
#Times360Malawi Bambo wa zaka 33, Steve Manda, wamangidwa poganizilidwa kuti amanamiza anthu kuti iye ndi msilikali wa Malawi Defence Force (MDF) wa ku Moyale Barracks ndipo amaberanso anthu, makamaka amayi. A Manda amangidwa dzulo madzulo pomwe bwenzi lawo linakawanenela ku polisi kuti lawabera K1.3 million . Malinga ndi mneneri wa polisi ya Jenda, a Macfarlen Mseteka, kafukufuku wawo wapeza kuti a Manda ananamiza mkaziyu kuti ndi msilikali ndipo iwo anagwa nawo mchikondi. Kutsatira izi, a Manda anawuza mayiyo kuti akufuna K1.3 million yoti akonzetsere galimoto yawo imene inaonongeka m'Chikangawa. A Mseteka ati mkaziyu anazazindikira kuti oganizilidwayu amagwiritsa ntchito njira imeneyi
No comments:
Post a Comment